1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Ine ndine Yehova Molungu wanu.
3. Musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Aigupto muja munakhalamo; musamacita monga mwa macitidwe a dziko la Kanani kumene ndipita nanuko, nimusamayenda m'malemba ao.