Levitiko 15:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo munthu ali yense wakukhudza kama wace azitsuka zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo,

6. Ndipo iye wakukhalira cinthu ciri conse adacikhalira wakukhayo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

7. Ndipo iye wakukhudza thupi la uyo wakukhayo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

8. Ndipo wakukhayo akalabvulira wina woyera; pamenepo atsuke zobvala zace, nasambe m'madzi, nadzakhala wodetsedwa kufikira madzulo.

Levitiko 15