Hoseya 12:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndiye Mkanani, m'dzanja lace muli miyeso yonyenga, akonda kusautsa.

8. Ndipo Efraimu anati, Zedi ndasanduka wolemera, ndadzionera cuma m'nchito zonse ndinazigwira; sadzapeza mwa ine mphulupulu yokhala cimo.

9. Koma Ine ndine Yehova Mulungu wako cicokere dziko la Aigupto, ndidzakukhalitsanso m'mahema, monga masiku a masonkhano oikika.

Hoseya 12