Hoseya 1:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. MAU a Yehova amene anadza kwa Hoseya mwana wa Beeri masiku a Uziya, Yotamu, Ahazi, ndi Hezekiya, mafumu a Yuda, ndi masiku a Yerobiamu mwana wa Yoasi mfumu ya Israyeli.

2. Ciyambi ca kunena kwa Yehova mwa Hoseya, Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, Muka, udzitengere mkazi wacigololo ndi ana acigololo; pakuti dziko latsata cigololo cokha cokha kuleka kutsata Yehova.

3. Ndipo anamuka natenga Gomeri mwana wamkazi wa Diblaimu; iye naima, nambalira mwana wamwamuna.

Hoseya 1