Genesis 43:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Amunawo ndipo anatenga mphatso, natenga ndalama zowirikiza m'manja mwao, ndi Benjamini; ndipo ananyamuka ndi kutsikira ku Aigupto, naima pamaso pa Yosefe.

16. Ndipo pamene anaona Benjamini pamodzi nao, anati kwa tsanyumba wace, Lowa nao anthuwo m'nyumba, kaphere iwo, kakoozere, cifukwa anthuwo adzadya ndi ine usana uno.

17. Munthuyo anacita monga anamuuza Yosefe, ndipo munthuyo analowa nao anthuwo m'nyumba ya Yosefe.

18. Anthuwo ndipo anaopa, cifukwa analowezedwa m'nyumba ya Yosefe; nati, Cifukwa ca ndalama zila zinabwezedwa m'matumba athu nthawi yoyamba ija, ife tilowezedwa, kuti aone cifukwa ndi ife, atigwere ife, atiyese ife akapolo, ndi aburu athu.

Genesis 43