Genesis 39:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo panali, nthawi yomweyo, iye analowa m'nyumba kuti agwire nchito yace; ndipo munalibe amuna a m'nyumba m'katimo.

12. Ndipo mkazi anagwira iye copfunda cace, nati, Gona ndi ine; ndipo anasiya copfunda cace m'dzanja lace nathawa, naturukira kubwalo.

13. Ndipo panali pamene mkazi anaona kuti anasiya copfunda cace m'dzanja lace, nathawira kubwalo,

14. anaitana amuna a m'nyumba yace, nanena ndi iwo kuti, Taonani, walowetsa kwa ife Mhebri kuti atiseke ife, analowa kwa ine kugona ndi ine, ndipo ndinapfuula ndi mau akuru:

15. ndipo panali pamene iye anamva kuti ndinakweza mau anga ndi kupfuula, iye anasiya copfunda cace kwa me nathawira kubwalo.

Genesis 39