30. Ndipo anabwera kwa abale ace, nati, Mwana palibe; ndipo ine ndipita kuti?
31. Ndipo anatenga malaya ace a Yosefe, napha tonde, nabvika malaya m'mwazi wace:
32. natumiza malaya amwinjiro, nadza nao kwa atate ao: ndipo anati, Siwa tawatola; muzindikire tsono ngati ndi malaya a mwana wanu, kapena ndi ena.
33. Ndipo anazindikira nati, Ndiwo malaya a mwana wanga: wajiwa ndi cirombo: Yosefe wakadzulidwa ndithu.