Genesis 35:13-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Mulungu anakwera kumcokera iye kumene ananena naye.

14. Ndipo Yakoboanaimiritsamwala pamalo pamene ananena ndi iye, coimiritsa camwala: ndipo anathira pamenepo nsembe yothira, nathirapo mafuta.

15. Ndipo anacha dzina lace la pamalo pamene Mulungu ananena ndi iye, Beteli.

16. Ndipo anacokera ku Beteli: ndipo panatsala nthawi asanafike ku Efrati: ndipo Rakele anabala nabvutidwa.

17. Ndipo panali pamene anabvutidwa, namwino anati kwa iye, Usaope: pakuti udzakhala ndi mwana wina wamwamuna.

18. Ndipo pakutsirizika iye, pakuti anamwalira, anamucha dzina lace Benoni; koma atate wace anamucha Benjamini.

19. Ndipo anafa Rakele, naikidwa pa njira va ku Efrati (ndipo Betelehemu),

Genesis 35