Genesis 32:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anagona komweko usiku womwewo, natengako zimene anali nazo, mphatso yakupatsa Esau mkuru wace:

14. mbuzi zazikazi mazana awiri, atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi mazana awiri, ndi zazimuna makumi awiri,

15. ngamila zamkaka makumi atatu ndi ana ao, ng'ombe zazikazi makumi anai, zazimuna khumi, aburu akazi makumi awiri ndi ana khumi.

16. Ndipo anazipereka zimenezo m'manja a anyamata ace, gulu pa lokha gulu pa lokha: ndipo anati kwa anyamata ace, Taolokani patsogolo panga, tacitani danga pakati pa magulu, tina ndi lina.

Genesis 32