62. Ndipo Isake anadzera njira ya Beereahai-roi; cifukwa kuti anakhala iye n'dziko la kumwera.
63. Ndipo Isake anaturuka kulingalira m'munda madzulo; ndipo anatukula maso ace, nayang'ana, taona, ngamila zinalinkudza,
64. Ndipo Rebeka anatukula maso ace, ndipo pamene anaonalsake anatsika pa ngamila,
65. Ndipo anati kwa mnyamata, Munthuyo ndani amene ayenda m'munda kukomana ndi ife? Mnyamatayo ndipo anati, Uyo ndi mbuyanga: cifukwa cace namwali anatenga cophimba cace nadziphimba.
66. Mnyamatayo ndipo anamuuza Isake zonse anazicita.