Genesis 2:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. ndipo nthitiyo anaicotsa Yehova Mulungu mwa Adamu anaipanga mkazi, ndipo ananka naye kwa Adamu.

23. Ndipo anati Adamu, Uyu tsopano ndiye pfupa la mafupa anga, ndi mnofu wa mnofu wanga; ndipo adzachedwa Mkazi, cifukwa anamtenga mwa mwamuna.

24. Cifukwa cotero mwamuna adzasiya atate wace ndi amace nadzadziphatika kwa mkazi wace: ndipo adzakhala thupi limodzi.

25. Onse awiri ndipo anali amarisece, mwamuna ndi mkazi wace, ndipo analibe manyazi.

Genesis 2