19. Ndipo anamdalitsa iye, nati, Abramu adalitsike ndi Mulungu Wamkurukuru, mwini kumwamba ndi dziko lapansi;
20. ayamikike Mulungu Wamkurukuru amene wapereka adani ako m'dzanja lako. Ndipo anampatsa iye limodzi la magawo khumi la zonse.
21. Mfumu ya Sodomu ndipo inati kwa Abramu, Ndipatse ine anthu, nutenge cuma iwe wekha.
22. Ndipo Abramu anati kwa mfumu ya Sodomu, Dzanja langa ndamtukulira Yehova, Mulungu Wamkurukuru, mwini kumwamba ndi dziko lapansi,