Ezekieli 5:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, udzitengere mpeni wakuthwa, ndiwo lumo la wometa, udzitengere ndi kulipititsa pamutu pako ndi pa ndebvu zako; nudzitengere muyeso kuyesa nao, ndi kugawa tsitsilo.

2. Limodzi la magawo ace atatu utenthe ndi moto pakati pa mudzi pakutha masiku a kuzingidwa mudzi, nutenge gawo lina ndi kukwapula-kwapula ndi lupanga pozungulira pace, nuwaze kumphepo gawo lotsala; pakuti ndidzasolola lupanga lakuwatsata.

3. Utengekonso owerengeka ndi kuwamanga m'mkawo wa maraya ako.

4. Nutengekonso pa amenewa ndi kuwaponya pakati pa moto, ndi kuwatentha m'moto; kucokera kumeneko udzaturuka moto pa nyumba yonse ya Israyeli.

5. Atero Yehova Mulungu, Uwu ndi Yerusalemu ndinauika pakati pa amitundu, ndi pozungulira pace pali maiko.

Ezekieli 5