34. ku mbali ya kumadzulo zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zace zitaru; cipata cimodzi ca Gadi, cipata cimodzi ca Aseri, cipata cimodzi ca Nafitali.
35. Pozungulira pace ndipo mabango zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ndi dzina la mudziwo kuyambira tsiku ilo lidzakhala, Yehova ali pomwepo.