Ezekieli 46:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo polowa kalonga azilowera njira ya ku khonde la cipata, naturuke njira yomweyo.

9. Koma pofika anthu a m'dziko pamaso pa Yehova m'madyerero oikika, iye amene alowera njira ya ku cipata ca kumpoto kudzalambira, aturukire njira ya ku cipata ca kumwera; ndi iye amene alowera njira ya ku cipata ca kumwera, aturukire njira ya ku cipata ca kumpoto; asabwerere njira ya cipata anadzeraco, koma aturukire m'tsogolo mwace.

10. Kalongayo tsono, polowa iwo alowe pakati pao, ndipo poturuka iwo aturukire pamodzi.

11. Ndi pamadyerero, ndi pa masiku opatulika, nsembe yaufa ikhale ya efa wa pa ng'ombe, ndi efa wa pa nkhosa yamphongo, ndi pa ana a nkhosa, monga akhoza kupatsa; ndi hini wa mafuta wa paefa.

Ezekieli 46