Ezekieli 40:45-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

45. Ndipo anati kwa ine, Kanyumba aka koloza kumwela nka ansembe odikira kacisi.

46. Ndi kanyumba koloza kumpoto nka ansembe odikira guwa la nsembe, ndiwo ana a Zadoki amene ayandikira kwa Yehova mwa ana a Levi, kumtumikira Iye.

47. Ndipo anayesa bwalolo mikono zana m'litali mwace, ndi mikono zana kupingasa kwace, lamphwamphwa; ndi guwa la nsembe linali kukhomo kwa nyumba.

48. Pamenepo anadza nane ku khonde la kacisi, nayesa mphuthu za khonde, mikono isanu cakuno, ndi mikono isanu cauko; ndi kupingasa kwa cipata, mikono itatu cakuno, ndi mikono itatu cauko.

49. M'litali mwace mwa khonde mikono makumi awiri, ndi kupingasa kwace mikono khumi ndi umodzi; ndipo panali makwerero khumi okwerera kumeneko; ndipo panali zoimiritsa pa nsanamirazo, imodzi cakuno, ndi imodzi cauko.

Ezekieli 40