Ezekieli 4:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo iwe wobadwa ndi munthu, dzitengere njerwa, nulike pamaso pako, nulembepo mudzi, ndiwo Yerusalemu;

2. nuuzinge, nuumangire nsanja zouzinga, nuundire nthumbira, ndi kuumangira misasa, nuuikire zogumulira pozungulira pace.

3. Nudzitengere ciwaya cacitsulo, ndi kuciika ngati khoma lacitsulo pakati pa iwe ndi mudziwo; nuulozetsere nkhope yako kuti umangidwire misasa, ndipo udzamangira misasa. Ici cikhale cizindikilo ca nyumba ya Israyeli.

Ezekieli 4