Ezekieli 3:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Pamenepo unandilowa mzimu ndi kundiimika ndikhale ciriri; ndipo analankhula ndi ine, nanena nane, Muka, katsekedwe m'nyumba mwako.

25. Koma iwe wobadwa ndi munthu, taona, adzakuikira iwe zingwe zolimba, nadzakumanga nazo, ndipo sudzaturuka pakati pao;

26. ndipo ndidzamamatiritsa lilime lako ku malakalaka ako, kuti ukhale wosanena, wosawakhalira wakuwadzudzula; pakuti iwo ndiwo nyumba yopanduka.

27. Koma pamene ndilankhula nawe ndidzatsegula pakamwa pako, nudzanena nao, Atero Yehova Mulungu. Wakumvera amvere, wasafuna kumvera akhale; pakuti iwo ndiwo nyumba yopanduka.

Ezekieli 3