5. Koma Ohola anacita cigololo pamene anali wanga, anaumirira mabwenzi ace Aasuri oyandikizana naye;
6. obvala cibakuwa, ziwanga, ndi akazembe, onsewo anyamata ofunika, anthu oyenda pa akavalo.
7. Ndipo anacita nao zigololo zace, ndiwo anthu osankhika a ku Asuri onsewo, ndipo ali onse anawaumirira anadziipsa nao mafano ao.
8. Sanalekanso zigololo zace zocokera ku Aigupto, pakuti anagona naye m'unamwali wace, nakhudza maere a unamwali wace, namtsanulira cigololo cao.
9. Cifukwa cace ndampereka m'dzanja la mabwenzi ace, m'dzanja la Aasuri amene anawaumirira.