36. Monga ndinaweruza makolo anu m'cipululu ca dziko la Aigupto, momwemo ndidzaweruza inu, ati Ambuye Yehova.
37. Ndipo ndidzakupititsani pansi pa ndodo ya mbusa ndi kukulowetsani m'cimango ca cipangano;
38. ndipo ndidzasankhula mwa inu opanduka ndi ondilakwira, ndidzawaturutsa m'dziko logoneramo iwo; koma sadzalowa m'dziko la Israyeli; motero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
39. Ndipo inu, nyumba ya Israyeli, atero Ambuye Yehova, mukani, tumikirani yense mafano ace, ndi m'tsogolo momwe, popeza simundimvera Ine; koma musaipsanso dzina langa lopatulika ndi zopereka zanu ndi mafano anu.
40. Pakuti pa phiri langa lopatulika, pa phiri lothubvuka la Israyeli, ati Ambuye Yehova, pomwepo onse a nyumba ya Israyeli, onsewo adzanditumikira Ine m'dzikomo; pomwepo ndidzawalandira, ndi pomwepo ndidzafuna nsembe zanu zokweza, ndi zoyamba za msonkho wanu, pamodzi ndi zopatulika zanu zonse.