Ezekieli 18:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. napereka molira phindu, nalandira coonjezerapo; adzakhala ndi moyo uyu kodi? sadzakhala ndi moyo, anacita zonyansa izi zonse; kufa adzafadi, niwazi wace umkhalira.

14. Taona tsono, yemweyo akabala mwana uyu, naona zocimwa zonse adazicita atate wace, naopa wosacita zoterezo,

15. wosadya pamapiri, kapena kukweza maso ace ku mafano a nyumba ya Israyeli, wosaipsa mkazi wa mnansi wace,

16. kapena kusautsa wina ali yense, wosatenga cigwiriro, wosatenga zofunkha; koma anapatsa wanjala cakudya cace, nabveka wamarisece ndi cobvala,

17. naletsa dzanja lace pa wozunzika, wosalandira phindu kapena coonjezerapo, wocita maweruzo anga, nayenda m'malemba anga; uyu sadzafera mphulupulu ya atate wace, adzakhala ndi moyo ndithu.

Ezekieli 18