22. Popeza mwamvetsa cisoni ndi mabodza mtima wa wolungama, amene sindinamvetsa cisoni Ine, ndi kumlimbitsa manja woipa, kuti asabwerere kuleka njira yace yoipa, ndi kusungidwa wamoyo;
23. cifukwa cace simudzaonanso zopanda pace, kapena kupenda; koma ndidzalanditsa anthu anga m'manja mwanu; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.