Ezekieli 13:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Popeza, inde popeza asokeretsa anthu anga, ndi kuti, Mtendere, pokhala palibe mtendere; ndipo anthu akamanga linga, aneneriwo alimata ndi dothi losapondeka;

11. uziti nao olimata ndi dothi losapondeka, kuti lidzagwa, lidzabvumbidwa ndi mvula yaikuru; ndi inu, matalala akuru, mudzagwa; ndi mkuntho udzalithithimula.

12. Ndipo taonani, litagwa linga, sadzanena nanu kodi, Liri kuti dothi munalimata nalo?

Ezekieli 13