Estere 8:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsiku lomwelo mfumu Ahaswero anampatsa mkazi wamkuru Estere nyumba ya Hamani mdani wa Ayuda, Nafika Moredekai pamaso pa mfumu; pakuti Estere adamuuza za cibale cace.

2. Ndipo mfumu inabvula mphete yace adailanda kwa Hamani, naipereka kwa Moredekai. Ndi Estere anaika Moredekai akhale woyang'anira nyumba ya Hamani.

3. Nanenanso Estere pamaso pa mfumu, nagwa ku mapazi ace, nalira misozi, nampembedza kuti acotse coipaco ca Hamani wa ku Agagi, ndi ciwembu adacipangira Ayuda,

4. Ndipo mfumu inaloza Estere ndi ndodo yacifumu yagolidi. Nanyamuka Estere, naima pamaso pa mfumu.

Estere 8