26. M'dziko la Goseni mokha, mokhala ana a Israyeli, munalibe matalala.
27. Ndipo Farao anatumiza, naitana Mose ndi Aroni, nanena nao, Ndacimwa tsopano; Yehova ndiye wolungama, ine ndi anthu anga ndife oipa,
28. Pembani kwa Yehova; cifukwa akwanira ndithu mabingu a Mulungu ndi matalala; ndipo ndidzakulolani mumuke, osakhalanso.