24. Ndipo kunali panjira, kucigono, Yehova anakomana naye, nafuna kumupha.
25. Koma Zipora anatenga mpeni wamwala, nadula khungu la mwana wace, naliponya pa mapazi ace; nati, Pakuti iwe ndiwe mkwati wanga wamwazi. Ndipo iye anamleka.
26. Pamenepo anati mkaziyo, Mkwati wamwazi iwe, cifukwa ca mdulidwe.
27. Ndipo Yehova ananena ndi Aroni, Muka kucipululu kukakomana ndi Mose. Ndipo anamuka, nakomana naye pa phiri la Mulungu, nampsompsona.