Eksodo 21:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Iye wakuba munthu, angakhale wamgulitsa, kapena akampeza m'dzanja lace, aphedwe ndithu.

17. Munthu wakutemberera atate wace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

18. Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzace ndi mwala, kapena ndi nkhonyo, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;

19. akaukanso, nakayendayenda pabwalo ndi ndodo yace, womkanthayo azikhala womasuka; pakutsotsa pace pokha azimbwezera, namcizitse konse.

20. Munthu akakantha mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, ndi ndodo, ndipo akafa padzanja pace; ameneyo aliridwe ndithu.

21. Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalirike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wace.

Eksodo 21