Eksodo 18:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. nati kwa Mose, Ine mpongozi wako Yetero ndadza kwa iwe, ndi mkazi wako, ndi ana ace omwe awiri.

7. Ndipo Mose anaturuka kukakomana ndi mpongozi wace, nawerama, nampsompsona; nafunsana ali bwanji, nalowa m'hema.

8. Ndipo Mose anafotokozera mpongozi wace zonse Yehova adazicitira Farao ndi Aaigupto cifukwa ca Israyeli; ndi mabvuto onse anakomana nao panjira, ndi kuti Yehova adawalanditsa.

9. Ndipo Yetero anakondwera cifukwa ca zabwino zonse Yehova adazicitira Israyeli, ndi kuwalanditsa m'dzanja la Aaigupto.

10. Nati Yetero, Woyamikika Yehova, amene anakulanditsani m'dzanja la Aaigupto, ndi m'dzanja la Farao; ameneanalanditsa anthu awa pansi pa dzanja la Aaigupto.

Eksodo 18