Eksodo 12:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo azitengako mwazi, naupake pa mphuthu za mbali ndi ya pamwamba m'nyumba zimene adyeramo.

8. Ndipo azidya nyamayo usiku womwewo, yooca pamoto, ndi mkate wopanda cotupitsa; aidye ndi ndiwo zowawa,

9. Musaidya yaiwisi, kapena yophika ndi madzi konse ai, koma yooca pamoto; muti wace ndi miyendo yace ndi matumbo ace.

10. Ndipo musasiyako kufikira m'mawa; koma yotsalira kufikira m'mawayo muipsereze ndi moto:

11. Ndipo muziidya cotero: okwinda m'cuuno, nsapato zanu pa mapazi anu ndodo yanu m'dzanja lanu, ndipo muziidya msanga; ndiye Paskha wa Yehova.

12. Pakuti ndidzapita pakati pa dziko la Aigupto usiku womwewo, ndi kukantha ana oyamba onse m'dziko la Aigupto, anthu ndi zoweta; ndipo ndidzacita maweruzo pa milungu yonse ya Aigupto; Ine ndine Yehova.

Eksodo 12