Deuteronomo 7:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. musamawaopa; mukumbukile bwino cimene Yehova Mulungu wanu anacitira Farao, ndi Aigupto wonse;

19. mayesero akuru maso anu anawapenya, ndi zizindikilo ndi zozizwa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, zimene Yehova Mulungu wanu anakuturutsani nazo; Yehova Mulungu wanu adzatero nayo mitundu yonse ya anthu imene muwaopa.

20. Komanso Yehova Mulungu wanu adzatumiza mabvu pakati pao, kufikira ataonongeka otsalawo, ndi akubisala pamaso panu.

21. Musamaopa pamaso pao; popeza Yehova Mulungu wanu ali pakati pa inu, Mulungu wamkuru ndi woopsa.

Deuteronomo 7