Deuteronomo 31:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo kudzakhala, zitawafikira zoipa ndi zobvuta zambiri, nyimbo iyi idzacita mboni pamaso pao; popeza siidzaiwalika m'kamwa mwa mbeu zao; popeza ndidziwa zolingirira zao azicita lero lino, ndisanawalowetse m'dziko limene ndinalumbira.

22. Potero Mose analembera nyimboyi tsiku lomweli, naiphunzitsa ana a Israyeli.

23. Ndipo anauza Yoswa mwana wa Nuni, nati, Khala wamphamvu, nulimbe mtima; pakuti udzalowa nao ana a Israyeli m'dziko limene ndinawalumbirira: ndipo Ine ndidzakhala ndi iwe.

24. Ndipo kunali, Mose atatha kulembera mau a cilamulo ici m'buku, kufikira atalembera onse,

25. Mose anauza Alevi akunyamula likasa la cipangano la Yehova, ndi kuti,

Deuteronomo 31