17. Koma azibvomereza wobadwa woyamba, mwana wa wodana naye, ndi kumwirikizira gawo lace la zace zonse; popeza iye ndiye ciyambi ca mphamvu yace; zoyenera woyamba kubadwa nzace.
18. Munthu akakhala naye mwana wamwamuna wopulukira, ndi wopikisana naye, wosamvera mau a atate wace, kapena mau a mai wace, wosawamvera angakhale anamlanga;
19. azimgwira atate wace ndi mai wace, ndi kuturukira naye kwa akuru a mudzi wace, ndi ku cipata ca malo ace;
20. ndipo anene kwa akulu a mudzi wace, Mwana wathu wamwamuna uyu ngwopulukira ndi wopikisana nafe, wosamvera mau athu, ndiye womwazamwaza, ndi woledzera.
21. Pamenepo amuna onse a mudzi wace amponye miyala kuti afe; cotero mucotse coipaco pakati panu; ndipo Israyeli wonse adzamva, nadzaopa.