Deuteronomo 19:8-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Yehova Mulungu wanu akakulitsa malire anu, monga analumbirira makolo anu, ndi kukupatsani dziko lonse limene ananena kwa makolo anu kuwapatsa ili;

9. ukadzasunga lamulo ili lonse kulicita, limene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kuyenda m'njira zace masiku onse; pamenepo mudzionjezere midzi itatu yina pamodzi ndi itatu iyi;

10. kuti angakhetse mwazi wosacimwa pakati pa dziko lanu, limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu, pangakhale mwazi pa inu.

11. Koma munthu akamuda mnzace, namlalira, ndi kumuukira ndi kumkanth a moyo wace, kuti wafa; nakathawira ku wina wa midzi iyi;

12. pamenepo akuru a mudzi wace atumize ndi kumtengako ndi kumpereka m'manja mwa wolipsa mwazi, kuti afe.

13. Diso lanu lisamcitire cifundo, koma mucotse mwazi wosacimwa m'Israyeli, kuti cikukomereni.

Deuteronomo 19