17. pamenepo anthu onse awiri, pakati pao pali makaniwo, aziima pamaso pa Yehova, pamaso pa ansembe ndi oweruza okhala m'masiku awa;
18. ndipo oweruza afunsitse bwino; ndipo taonani, mboniyo ikakhala mboni yonama, yomnamizira mbale wace;
19. mumcitire monga iye anayesa kumcitira mbale wace; motero mucotse coipaco pakati panu.
20. Ndipo otsalawo adzamva, nadzaopa, ndi kusacitanso monga coipaco pakati panu.