19. Musamapotoza ciweruzo, musamasamalira munthu, kapena kulandira cokometsera mlandu; popeza cokometsera mlandu cidetsa maso a anzeru, niciipsa mau a olungama.
20. Cilungamo, cilungamo ndico muzicitsata, kuti mukhale ndi moyo ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.
21. Musamadziokera mitengo iri yonse ikhale nkhalango pafupi pa guwa la nsembe la Yehova Mulungu wanu, limene mwadzimangira.
22. Ndipo musamadziutsira coimiritsa ciri conse cimene Yehova Mulungu wanu adana naco.