Deuteronomo 15:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakutha Pace pa zaka zisanu ndi ziwiri pakhale cilekerero.

2. Cilekereroco ndici: okongoletsa onse alekerere cokongoletsa mnansi wace; asacifunse kwa mnansi wace, kapena mbale wace; popeza analalikira cilekerero ca Yehova.

3. Muyenera kucifunsa kwa mlendo; koma canu ciri conse ciri ndi mbale wanu, dzanja lanu licilekerere;

4. ndiko kuti pasakhale waumphawi mwa inu; pakuti Yehova adzakudalitsani kwambiri m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale colowa canu canu;

5. cokhaci mumvere cimverere mau a Yehova Mulungu wanu, kuti musamalire kucita malamulo awa onse amene ndikuuzani lero lino.

6. Popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani, monza ananena nanu; ndipo mudzakongoletsa amitundu ambiri, osakongola nokha; nimudzacita ufumu pa amitundu ambiri, koma iwo sadzacita ufumu pa inu.

Deuteronomo 15