17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.
18. Ndipo m'mene analikulankhula ndi ine ndinagwidwa ndi tulo tatikuru, nkhope yanga pansi; koma anandikhudza, nandiimiritsa pokhala inepo,
19. Ndipo anati, Taona, ndidzakudziwitsa cimene cidzacitika pa citsiriziro ca mkwiyowo; pakuti pa nthawi yoikika mpakutha pace,
20. Nkhosa yamphongo waiona ya nyanga ziwiri ndizo mafumu a Mediya ndi Perisiya.
21. Ndi tonde wamanyenje ndiye mfumu ya Helene, ndi nyanga yaikuru iri pakati pa maso ace ndiyo mfumu yoyamba.