Danieli 8:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.

18. Ndipo m'mene analikulankhula ndi ine ndinagwidwa ndi tulo tatikuru, nkhope yanga pansi; koma anandikhudza, nandiimiritsa pokhala inepo,

19. Ndipo anati, Taona, ndidzakudziwitsa cimene cidzacitika pa citsiriziro ca mkwiyowo; pakuti pa nthawi yoikika mpakutha pace,

20. Nkhosa yamphongo waiona ya nyanga ziwiri ndizo mafumu a Mediya ndi Perisiya.

21. Ndi tonde wamanyenje ndiye mfumu ya Helene, ndi nyanga yaikuru iri pakati pa maso ace ndiyo mfumu yoyamba.

Danieli 8