Danieli 8:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo ndinamva mau a munthu pakati pa magombe a Ulai, naitana, nati, Gabrieli, zindikiritsa munthuyu masomphenyawo.

17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.

18. Ndipo m'mene analikulankhula ndi ine ndinagwidwa ndi tulo tatikuru, nkhope yanga pansi; koma anandikhudza, nandiimiritsa pokhala inepo,

19. Ndipo anati, Taona, ndidzakudziwitsa cimene cidzacitika pa citsiriziro ca mkwiyowo; pakuti pa nthawi yoikika mpakutha pace,

Danieli 8