15. Ndipo kunali, nditaona masomphenyawo, ine Danieli ndinafuna kuwazindikira; ndipo taonani, panaima popenyana ndi ine ngati maonekedwe a munthu.
16. Ndipo ndinamva mau a munthu pakati pa magombe a Ulai, naitana, nati, Gabrieli, zindikiritsa munthuyu masomphenyawo.
17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.