Danieli 7:15-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Koma ine Danieli, mzimu wanga unalaswa m'kati mwa thupi langa, ndi masomphenya a m'mtima mwanga anandibvuta.

16. Ndinayandikira kwa wina wa iwo akuimako ndi kumfunsa za coonadi za ici conse. Ndipo ananena nane, nandidziwitsa kumasulira kwace kwa zinthuzi:

17. Zirombo zazikuru izi zinai ndizo mafumu anai amene adzauka pa dziko lapansi.

Danieli 7