Danieli 6:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kudamkomera Dariyo kuikira ufumuwo akalonga zana limodzi mphambu makumi awiri akhale m'madera onse a ufumu;

2. ndi akuyang'anira iwo akulu atatu, woyamba wao ndi Danieli; kuti akalonga awa adziwerengere kwa iwo, ndi kuti za mfumu zisasoweke.

3. Pamenepo Danieli amene anaposa akuluwa ndi akalonga, popeza munali mzimu wopambana mwa iye, ndi mfumu inati imuike woyang'anira ufumu wonse.

Danieli 6