3. Ha! zizindikilo zace nzazikuru, ndi zozizwa zace nza mphamvu, ufumu wace ndiwo ufumu wosatha, ndi kulamulira kwace ku mibadwo mibadwo.
4. Ine Nebukadinezara ndinalimkupumula m'nyumba mwanga, ndi kukhala mwaufulu m'cinyumba canga,
5. Ndinaona loto lakundiopsa, ndi zolingilira za pakama panga, ndi masomphenya a m'mtima mwanga, zinandibvuta ine.
6. Cifukwa cace ndinalamulira kuti adze kwa ine anzeru onse a ku Babulo, kuti andidziwitse kumasulira kwace kwa lotoli.