Danieli 3:17-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Taonani, Mulungu wathu amene timtumikira akhoza kutilanditsa m'ng'anjo yotentha yamoto, nadzatilanditsa m'dzanja lanu, mfumu.

18. Koma akapanda kutero, dziwani, mfumu, kuti sitidzatumikira milungu yanu, kapena kulambira fano lagolidi mudaliimikalo.

19. Pamenepo Nebukadinezara anadzazidwa ndi ukali, ndi maonekedwe a nkhope yace anasandulikira Sadrake, Mesake, ndi Abedinego; anayankha, nati asonkheze ng'anjo kasanu ndi kawiri koposa umo amasonkhezera.

20. Nauza amuna ena amphamvu a m'khamu lace la nkhondo amange Sadrake, Mesake, ndi Abedinego, ndi kuwaponya m'ng'anjo yotentha yamoto.

Danieli 3