36. Ili ndi loto; kumasulira kwace tsono tikufotokozerani mfumu.
37. Inu mfumu ndinu mfumu ya mafumu, pakuti Mulungu wa Kumwamba anakupatsani ufumu, ndi mphamvu yaikuru, ndi ulemu;
38. ndipo pali ponse pokhala ana a anthu Iye anapereka nyama za kuthengo, ndi mbalame za m'mlengalenga, m'dzanja lanu; nakucititsani ufumu pa izi zonse; inu ndinu mutuwo wagolidi.
39. Ndi pambuyo pa inu padzauka ufumu wina wocepa ndi wanu, ndi ufumu wina wacitatu wamkuwa wakucita ufumu pa dziko lonse lapansi.