Danieli 11:18-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pambuyo pace adzatembenuzira nkhope yace kuzisumbu, nadzalanda zambiri; koma kalonga wina adzaleketsa kunyoza kwace adanyoza nako; inde adzambwezera yekha kunyoza kwace.

19. Pamenepo adzatembenuzira nkhope yace ku malinga a dziko lace lace; koma adzakhumudwa, nadzagwa osapezedwanso.

20. Ndipo m'malo mwace adzauka wina wakupititsa wamsonkho pa ulemerero wa ufumuwo; koma atatha masiku owerengeka adzatyoledwa iye, si mwamkwiyo, kapena kunkhondo ai.

21. Ndi m'malo mwace adzauka munthu woluluka, amene anthu sanampatsa ulemu wa ufumu, koma adzafika kacetecete, nadzalanda ufumu ndi mau osyasyalika.

22. Ndipo mwa mayendedwe ace a cigumula adzakokololedwa pamaso pace, nadzatyoledwa, ngakhale kalonga yemwe wa cipangano.

23. Ndipo atapangana naye adzacita monyenga; pakuti adzakwera, nadzasanduka wamphamvu ndi anthu owerengeka.

Danieli 11