1. Zitatha izi ndinapenya, ndipo taonani, khomo lotseguka m'Mwamba, ndipo mau oyamba ndinawamva, ngati lipenga Iakulankhuia ndi ine, anati, Kwera kuno, ndipo ndidzakuonetsa zimene ziyenera kucitika m'tsogolomo.
2. Pomwepo ndinakhala mwa Mzimu; ndipo, taonani padaikika mpando wacifumu m'Mwamba ndi pa mpandowo padakhala wina;
3. ndipo maonekedwe a iye wokhalapo anafanana ndi mwaia wa jaspi, ndi sardiyo; ndipo panali utawaleza wozinga mpando wacifumu, maonekedwe ace ngati smaragido.
4. Ndipo pozinga mpando yacifumu mipando yacifumu makumi awiri mphambu inai; ndipo pa mipandoyo padakhala akuru makumi awiri mphambu anai, atabvala zobvala zoyera, ndi pamitu pao akorona agolidi.