20. Komatu ndiri nako kotsutsana ndi iwe, cuti ulola mkazi 2 Yezebeli, wodzieha zekha mneneri; ndipo aphunzitsa, nasokeretsa akapolo anga, kuti acite cigololo ndi kudya zoperekedwa nsenbe kwa mafano.
21. Ndipo ndanpatsa iye nthawi kuti alape; koma safuna kulapa kusiyana naco cigololo cace.
22. Taona, ndimponya iye pakama, ndi iwo akucita cigololo naye kuwalonga m'cisautso cacikuru, ngati salapa iwo ndi kuleka nchito zace.
23. Ndipo ndidzaononga ana ace ndi imfa; ndipo idzazindikira Mipingo yonse kuti 3 ine ndine iye amene ayesa imso ndi mitima; ndipo 4 ndidzaninkha kwa yense wa inu monga mwa nchito zanu.
24. Koma ndinena kwa inu, kwa otsala a ku Tiyatira, onse amene alibe ciphunzitso ici, amene sanazindikira zakuya za Satana, monga anena, Sindikusanjikizani katundu wina.