10. Ndipo si cotero cokha, koma Rebekanso, pamene anali ndi pakati pa mmodzi, ndiye kholo lathu Isake;
11. pakuti anawo asanabadwe, kapena asanacite kanthu kabwino kapena koipa, kuti kutsimikiza mtima kwa Mulungu monga mwa kusankha kukhale, si cifukwa ca nchito ai, koma cifukwa ca wakuitanayo,
12. cotero kunanenedwa kwa uyo, Wamkuru adzakhala kapolo wa wamng'ono.