29. Kapena Mulungu ndiye wa Ayuda okha okha kodi? si wao wa amitundunso kodi? Bya, wa amitundunso:
30. ngatitu ndiye Mulungu mmodzi, amene adzawayesa amdulidwe olungama ndi cikhulupiriro, ndi akusadulidwa mwa cikhulupiriro,
31. Potero kodi lamulo tiyesa cabe mwa cikhulupiriro? Msatero ai; koma tikhazikitsa lamulo.