10. monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;
11. Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;
12. Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.
13. M'mero mwao muli manda apululu;Ndi lilime lao amanyenga; Ululu wa mamba uli pansi pa milomo yao;
14. M'kamwa mwao mudzala ndi zotemberera ndi zowawa;
15. Miyendo yao icita liwiro kukhetsa mwazi;
16. Kusakaza ndi kusauka kuli m'njira zao;
17. Ndipo njira ya mtendere sanaidziwa;
18. Kumuopa Mulungu kulibe pamaso pao.